Chimbudzi cha K15.9 million ku Rumphi chagwa

Chimbudzi cha ndalama zokwana K15.9 million chomwe khonsolo ya Rumphi inamanga pa nyumba yodikilira amayi apakati pa chipatala cha Rumphi chagwa masanawa.

Wapampando wa komiti ya zaumoyo pachipatalachi a Manase Mhango wati akukaikira kuti chimbudzichi chagwa kamba koti sichinamangidwe molimba.

 

A Mhango ati pakadali pano adziwisa kale DC wabomali za nkhaniyi ndipo ati palibe wavulala ndi ngoziyi.

 

Chimbudzichi chagwa patangodusa chaka chimodzi kuchokela pomwe khonsolo yabomali inachipeleka kwa amayi pachipatalachi kuti azichigwiritsa ntchito.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Malawi Court unfreezes K24 billion in Bilderberg bank accounts

The High Court in Malawi, the Commercial Division, has issued an order to unfreeze accounts for businessman William Bilderberg who...

Close