A Chakwera amazitamandira ndi ntchito zomwe zinayambika nthawi ya DPP, atero a Navicha
Mtsogoleri wa chipani cha DPP ku Nyumba ya Malamulo, Mary Navicha, wadzudzula boma la Tonse kamba kodzitamandira pa ntchito zachitukuko zomwe zidayambika panthawi yomwe DPP inali m’boma.
Izi zadza pomwe nduna zosiyanasiyana za mbali ya boma zimafotokoza zina mwa ntchito zachitukuko zomwe zikuchitika mdziko muno m’maboma osiyanasiyana.
Polankhula , Mary Navicha yemwe adasankhidwa kukhala mtsogoleri wachipani cha DPP posachedwapa, wadandaula kuti boma lalephera kumalizitsa ntchito zachitukuko munthawi yabwino ngakhale ndalama zomalizitsitsira zitukuko zi zidali zitaperekedwa kale DPP ili m’boma .
Kuonjezera apo, Navicha wati pakufunika kuti boma la tonse liyambe kuyamikila ntchito ndi maziko abwino omwe DPP idakhazikitsa mmbuyomu.