A Polisi ku Nathenje amenya woyimba wokalamba Jetu kunsana, watero Dorothy Shonga

Apolisi ku Lilongwe anamenya kumsana kwa oyimba Jetu, watero mmayi wazamalonda Dorothy Shonga yemwe amadziwika kwambiri kuti Cash Madam.
Wamenyedwa: Jetu
Izi zinatsatira kusamvana komwe kunabuka pomwe apolisi ndi ena aku nthambi yotelera msonkho ya MRA paza zikalata za galimoto ya Dorothy yomwe anthuwa amayendera.
Malingana ndi Shonga yemwe wati chipwilikitichi chinadza kuyambila malo achipikisheni a Nathenje pomwe anthuwa amapita ku Blantyre.
Mukulemba kwake Shonga anati apolisiwa samakhutira ndi momwe iwo amafotokozera za umboni oti galimotoyo ndi yawo.
Apolisi anawauzanso kuti lamulo silitengera kuti munthu ndi otchuka kapena ayi.
Kutsatira kusamvanako, Shonga wati mmodzi mwa ofesala anamenya Jetu kumsana yemwe watchuka ndi nyimbo yotchedwa Chakwaza.
Shonga waonetsa malingaliro okamang’ala pa nkhaniyi ponena kuti akukhulupilira kuti apolisi akudzidwa kuti awaphwanyira ufulu komanso awachititsa manyazi pagulu komanso kuwanamizila kuti anali ndi galimoto yopanda zilolezo ndinso kuphonya mwayi otchita ntchito yamalonda.

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Direct cash transfer of K214million distributed to over 500 families affected by floods in Nkhotakota.

International Federation of Red Cross (IFRC) and Danish Red Cross have through Malawi Red Cross Society made a distribution of...

Close