Aford yasindika kuti izayima payokha ndipo yanenetsa kuti izatenga upulezidenti wa dziko lino

Chipani cha Alliance for Democracy (Aford) chati chili ndi chikhulupiliro kuti chidzapambana chikadzaima pa chokha pa chisankho cha mtsogoleri wa dziko cha chaka cha mawa.

Maluwa: Aford njowinawina

Wofalitsa nkhani za chipanichi a Amatullah Annie Maluwa auza Nyasatimes kuti kwa zaka zitatu tsopano chipanichi chakula mphamvu zimene zikupereka chirimbikitso kuti chidzaime pa chokha.

A Maluwa ati kutuluka kwa anthu ena mchipanichi ndi chitsimikizo kuti m’chipanichi muli demokalase ndipo anthu ena akhale akulowanso mchipanichi.

Posachedwapa, amene adali mlembi wamkulu wa chipanichi a Elias Wakuda Kamanga adatuluka mchipanichi ndi kulowa chipani chomwe chidayambitsidwa kumene cha National Development Party chomwe chikusogozedwa ndi a Frank Mwenifumbo

Aford inkadzudzula a Kamanga kuti ankapanga ndale za umthira kuwiri zomwe iwo eni adakana.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
WHO advises countries to commit to 2023 UN declaration on TB

As the world continues advocacy to end Tuberculoisis (TB) the World Health Organization (WHO) has called for political commitments and...

Close