Ana sukulu pa Soche Technical achita ziwonesero kamba ati akungodya nyemba basi

Kwavuta ku Soche Technical College ku Blantyre komwe ana a sukulu akutseka misewu kamba kokwiya kuti miyezi ikudusa koma akungolandira zakudya zomwe ndiwo zake ndi nyemba basi.

Wachiwiri wa Student Union Council pa sukulupo a Tiyanjane Chisowire wati ndiwodandaula chifuwa ma sabata akwana anayi tsopano chitsegulire sukuluyi koma ndiwo zimangokhala nyemba basi.

Mtsogoleri wa sukuluyi panopa akuyesesa kuti akambirane ndi ana asukuluwa ndipo chigulu cha a Polisi chafika kale kuzathandizira kubweresa bata.

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Silver Strikers halts process of recruiting Peter Mponda as new coach: Fears he is still Bullets fan

Sponsors of Silver Strikers Football Club over the weekend halted the running process of recruiting a new coach, Peter Mponda,...

Close