Mphunzitsi adya ndalama za mayeso za ophunzira 30, akanika kulemba mayeso

Ophunzira 30 pa sukulu ya sekondare  ya Seven Hills pa Chimbiya ku Dedza salemba nawo mayeso a MANEB a Form 2 ndi Form 4   kaamba koti mphunzitsi wa mkulu pasukuluyi anawadyera ndalama zawo za mayeso .

Ena mwa ophunzirawa auza Zodiak kuti ndizokhumudwitsa kuti mtsogoleri wawo yemwe wawachita chipongwe.

Mwini wake wa sukukuyi  a Hawa Ibrahim watsimikiza za nkhaniyi powonjezera kuti mphunzitsiyu anasakaza ndalama za ophunzira 20 ndipo khumi analephera kulipira  ndalama ya mayeso.

Iwo ati nkhaniyi anakayitula ku polisi  komanso   analembera Kalata bungwe la MANEB ndipo anawauza kuti ndizosatheka kuti ophunzirawa alembe nawo mayeso a chaka chino.

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
World Bank impressed with Malawi government economic strides

The World Bank says Malawi has achieved incredible economic results in the last three months despite concerns on macroeconomic stability...

Close