Nankhumwa apempha boma liganizire omwe adasewerapo mpira wamiyendo ndi wa manja m’mbuyomu

Mtsogoleri wa zipani zotsutsa boma m’nyumba ya malamulo a Kondwani Nankhumwa omwenso ndi phungu wa dera la Mulanje Central, apempha unduna woona za masewero kuti uganizire anthu omwe adasewerapo mpira wa miyendo komanso wa manja m’mbuyomu.

Coach Yasin ‘Titch’ Osman, former Wanderers coach Kannock Munda, former Big zbullets ciach Gilbert Chirwa and former Malawi coach Kinnah Phiri photo by Jeromy Kadewere, Nyasa Times

A Nankhumwa ati n’zomvetsa chisoni kuona a namandwa ena omwe adasewerapo mpira bwino m’mbuyomu akuvutika kwambiri.

 

Mwachitsanzo a Nankhumwa ati akatswiri ena omwe adasewerapo mpira m’mbuyomu akukhala moyo wovuta ndipo ena akuchita kusowa ndalama yoti apitire kuchipatala.

 

Nduna yoona za masewero a Uchizi Mkandawire yati unduna wawo ukukonza ndondomeko yomwe idzidzathandiza akatswiri osewera mpira opuma komanso omwe adathandizira ntchito za masewero kuti zipite patsogolo ndipo posachedwa, alengeza momwe ndondomekoyi idzigwilira ntchito.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Its working! Israel remits K1.2 billion to Malawi under the labour export arrangement

Finance Minister Simplex Chithyola Banda has confirmed that 735,000 US dollars have been transferred to Malawi through the Israel Labour...

Close