Pakali pano tafikira anthu oposa 700 000 ndi chimanga chaulere, atero Bushiri

Prophet Shepherd Bushiri wati pakali pano ntchito yawo yogawa chimanga chaulere kwa a Malawi omwe akhuzidwa ndi ngozi zadzidzidzi yikupitilirabe ndipo panopa afikira anthu oposa 700 000.

Kusakala: Tafikira anthu oposa 700 000

Mneneri wa a Bushiri a Aubrey Kusakala anena izi ku Mangochi komwe athandiza mabanja oposa 200 mdera la Senior Chief Nankumba ku Monkey-Bay m’boma la Mangochi.

A Bushiri achita potsatira vuto lakusefukira kwa madzi lomwe lakhudza mabanja ankhaninkhani maka mbali mwanyanja mdziko muno.

Mneneri wa a Bushiri a Aubrey Kusakala ati potsatira vuto lomwe linagwera anthuwa, mmneneriyu anaganiza zothandiza anthuwa.

A Kusakala ati aka ndi kachitatu kugawa chimanga ku Mangochi ndipo pakadali pano ntchito yogawa chimanga chaulere ya chaka chino kwa anthu osowa mdziko muno yafikira anthu oposa 700,000.

Anthu ammaboma a Karonga, Nkhotakota, mzinda wa Mzuzu, Nkhatabay, Ntcheu Lilongwe, Nsanje, Mulanje, Thyolo ndi Zomba ndi omwe alandira nawo thandizoli.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
ATM Week: Sudan Mining Minister arrives in the country for the Mining Investment Forum starting Tuesday

The Minister of Mining in South Sudan, Martin Gama Abucha, has arrived together with his Under Secretary for the Ministry...

Close