Watulukira Gaddafi General Longwe! Akuti muvoteleni kuti a Malawi mulawe kusintha
Mzika ya dziko lino a Eddie Gaddafi General Longwe omwe amakhala mdziko la Asia ati alindichidwi chopikisana nawo pazisankho za mtsogoleri wadziko lino zomwe zikuyembekezeka kuchitika chaka chamawa ngati oyima pawokha.
Agadafi auza Nyasatimes kuti iwo ndiwokonzeka kuombola amalawi omwe pakadali pano akukumana ndimavuto osiyanasiyana mu ulamuliro wa presidenti Dr. Lazarus Chakwera.
Iwo ati ali ndinfundo zikuluzikulu zingapo zomwe akuti ndizothandiza kutukula dziko lino komaso miyoyo ya amalawi.
Zina mwamfundozi ndimonga kuthana ndikatangale, kulimbikitsa nkhani za ulimi ndikuti dziko lino likhale ndichakudya chokwanira, kulimbikitsa olamuliro wabwino, kulimbitsa chitetezo cha dziko komanso kutukula ntchito za umoyo m’magawo osiyanasiyana.
“Pali zambiri zomwe ndakonzekera kuwachitira amalawi anzanga. Azuzika kokwana ndipo nthawi yoti awomboledwe yakwana,” watero Longwe.
Kotero iye wapempha anthu kuti adzamuvotere mwa unyinji kuti masomphenya ake azakwanilitsidwe maka ofuna kutukula dziko lino.
Longwe anabadwira ndikukulira mchigawo chakumpoto kwadziko lino.
Bambo ake amachokera m’boma la Nkhotakota pomwe mayi ake amachoka m’boma la Mzimba.
Kunkhani zamaphunziro, Longwe ali ndi digli ya za business komaso diploma yokhudza makompyuta.
Trying your best is not a sin
Dziko la Asia?