A Mutharika akuti ali ndi mawu oti awawuza a Chakwera, atero a Namalomba

Mtsogoleri wa chipani cha DPP Peter Mutharika wati ali ndi mau omwe akufuna kumuuza mtsogoleri wa dziko lino yemweso ndi mtsogoleri wa chipani cha MCP Lazarus Chakwera lachitatu likudzali.

Afuna kuyankhulana

Mutharika wayankhula izi kudzera kwa mneneri wake Shadrick Namalomba.

 Poyankhula ndi atolankhani mdziko muno lero, Namalomba wati Mutharika ali ndi mau omwe akufuna kuuza Chakwera pa za kuvulazidwa kwa anthu otsatira DPP mu mzinda wa Lilongwe.

 “Ngakhale a Mutharika akhale akuyankhula ku mtundu wa a Malawi Lachitatu lino pa ziwawa-zi koma kweni kweni uthenga-wu udzakhala ukupita kwa a Chakwera, ” watero Namalomba.

 Namalomba wanena kuti ali ndi umboni ochuluka kuti chipani cha MCP ndi chomwe chavulaza otsatira DPP kaamba ka number plate ya galimoto yomwe inanyamula anthu-wo akuti mwini wake ndi wa MCP.

 Padakali pano chipani cha MCP chakana kuti sichikukhudzidwa pa zipolowezi.

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Youth activist Hoppings Masanga appeals to the youth to refrain from perpetrating violence

A youth activist in the country, Hoppings Chabwera Masanga has warned that youths in the country will continue being used...

Close