Tamia Ja amangidwa poganiziridwa kuti anazembeyesa K8 miliyoni ya mwini

Apolisi munzinda wa Lilongwe amanga mmodzi mwa anthu odziwika bwino pamasamba amchezo Hannah Jabes, yemwe amadziwika bwino ndi dzina la Tamia Ja, kamba kankhani yogwirizana ndi kuba.
Tamia Ja
Malingana ndi a polisi, masiku angapo apitawo analandira dandaulo kuchokera kwa mkulu wina wochita malonda yemwe anati Tamia Ja anazambayitsa ndalama zokwana 8 million kwacha zitaikidwa molakwika mu akaunti yake.
Poyankhula mneneri wa polisi ya Lingadzi Cassim Manda wati Tamia Ja poyamba anauza munthu yemwe anatumiza molakwika kuti walandiradi ndalamazi ndipo abweza koma panthawiyo anali paulendo wopita mdziko la South Africa.
Manda anawonjezera kunena kuti kuchokera nthawi imeneyo Tamia Ja anayamba zozembazemba kuti abweze ndalamazi mpakana pakadali pano wamangidwa ndi apolisi.

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Kamlepo ayambitsa phokoso ku Parliament atadzudzula boma kuti sililabadira anthu aku mpoto

Ku nyumba ya malamulo kunabuka chipwirikiti masanawa, zomwe zidapangitsa kuti Kamlepo Kalua, phungu wa dera la ku mmawa m'boma la...

Close