Zandikwana! Enock Chihana akuti amanga yekha chiliza cha abambo ake: Boma latinamiza mokwanira

Mtsogoleri wa Aford a Enock Chihana ati pa 6 April chaka chino akhala akukhazikitsq ntchito yomanga chiliza cha malemu Chakufwa Chihana omwe anali bambo ake. Iwo ati akulu akulu ena aku mabungwe monga a United Nations komanso mtsogoleri wakale wa dziko lino Dr Bakili Muluzi awalonjeza kuti akayamba ntchito yomanga chilizachi adzawathandiza.

Chihana:

Iwo alankhula izi pamwambo omwe achipani cha Aford anakonza olambula kumanda a malemu Chakufwa Chihana mu mzinda wa Mzuzu.

A Chihana ati mbuyomu akubanja samachita kanthu pankhani ya chiliza cha bambo awo kamba koti boma linalonjeza kuti limanga chiliza cha malemu Chakufwa Chihana.

“Ine ngati mwana oyamba wa a Chakufwa Chihana ndikupepesa akubanja onse kamba koti papita zaka 18 chiliza cholongosoka cha bambo awo chisanamangidwe”anatero a Chihana.

 

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Chakwera meets KK flood victims, condoles bereaved families and appeals for more support

President Dr Lazarus McCarthy Chakwera on Thursday consoled victims of the devastating floods in Nkhota Kota, assuring that his government...

Close