Kamlepo wakwiya, ati ngati boma lipitilize kukondera asamukira ku Tanzania

Phungu wadera lakumvuma kwa boma la Rumphi a Kamlepo Kalua wati ndiwokonzeka kukhala nzika ya dziko la Tanzania ngati boma lipitilize kupereka ntchito za chitukuko mokondera.

Kalua:

Polankhula mnyumba ya malamulo masanawa a Kalua ati mzodandaulitsa kuti boma likuyenera kukwanilitsa malonjezano ake pa nkhani ya chitukuko kudera lawo pofotokoza kuti kuli mavuto mavuto ambiri.

Iwo ati Malawi ndiwa aliyense ndipo boma la a Chakwera lisamaone mtundu wa anthu kapena dera potukula dziko lino

Koma mtsogoleri wa zokambilana mnyumbayi a Richard Chimwendo Banda wati mzokhumudwitsa kuti a Kalua alankhula motere kaamba koti boma lakwanilitsa ntchito zosiyanasiyana za chitukuko kudera lawo komanso madera ena osiyanasiyana.

Follow and Subscribe Nyasa TV :

Sharing is caring!

Follow us in Twitter
Read previous post:
Govt says it has reached out to 4.3 million hungry households so far with food

Minister of Information and Digitalization, Moses Kunkuyu, says President Lazarus Chakwera Government has reached out to 4.3 million people affected...

Close